Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Kodi Baibo Imakamba Ciani?

Kodi Baibo Imakamba Ciani?

Kodi Mulungu amayankha mapemphelo onse?

KODI MUNGAKAMBE KUTI AMAYANKHA MAPEMPHELO . . .

  • A munthu aliyense

  • A anthu ena

  • Sayankha

ZIMENE BAIBO IMAKAMBA

“Yehova ali pafupi ndi onse . . . amene amamuitana m’coonadi.”—Salimo 145:18.

MFUNDO ZINA ZIMENE BAIBO IMAKAMBA

  • Mulungu sayankha mapemphelo a anthu amene samumvela. (Yesaya 1:15) Koma anthu a conco ‘angakhalenso pa ubwenzi wabwino’ na Mulungu ngati asintha makhalidwe awo.—Yesaya 1:18.

  • Kuti Mulungu ayankhe pemphelo, lifunika kukhala logwilizana na zimene iye amafuna, ndipo zimene amafunazo zipezeka m’Baibo.—1 Yohane 5:14.

Kodi tifunika kukhala bwanji popemphela?

ANTHU ENA AMAKHULUPILILA kuti nthawi zonse tifunika kugwada, kuŵelama, kapena kuika manja pamodzi popemphela. Inu muganiza bwanji?

ZIMENE BAIBO IMAKAMBA

Mulungu anayankha mapemphelo a anthu amene anapemphela ali ‘cokhala pansi,’ ‘coimilila,’ ‘cogona’ kapena ‘cogwada.’ (1 Mbiri 17:16; 2 Mbiri 30:27; Ezara 10:1; Machitidwe 9:40) Iye safuna kuti tikhale mwanjila inayake yapadela popemphela.

MFUNDO ZINA ZIMENE BAIBO IMAKAMBA

  • Mulungu amamvela mapemphelo a anthu odzicepetsa.—Salimo 138:6.

  • Mungapemphele ca mumtima ndiponso m’cinenelo ciliconse.—2 Mbiri 6:32, 33; Nehemiya 2:1-6.