Kodi Ufumu wa Mulungu N’ciani?
Anthu ambili amapemphela kuti Ufumu wa Mulungu ubwele. Koma kodi munadzifunsapo kuti Ufumu wa Mulungu n’ciani? Nanga udzacita ciani?
ONANI ZIMENE BAIBO IMAKAMBA:
Kodi Ufumu wa Mulungu N’ciani?
Ni boma la kumwamba limene wolamulila wake ni Yesu Khristu monga Mfumu.—Yesaya 9:6, 7; Mateyu 5:3; Luka 1:31-33.
Kodi Ufumu wa Mulungu udzacita ciani?
Udzacotsapo zoipa zonse na kubweletsa mtendele wamuyaya kwa anthu padziko lapansi.—Danieli 2:44; Mateyu 6:10.
Kodi kufuna-funa Ufumu coyamba kumatanthauza ciani?
Kumatanthauza kucilikiza Ufumu wa Mulungu, na kukhulupilila kuti iwo wokha ndiwo udzakonza zinthu padziko lapansi kuti zikhale mmene Mulungu amafunila.—Mateyu 6:33; 13:44.