Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Kodi Mboni za Yehova Zimakhulupilila Ciani?

Kodi Mboni za Yehova Zimakhulupilila Ciani?

Mboni za Yehova zimakhulupilila kuti “Malemba onse anauzilidwa ndi Mulungu, ndipo ndi opindulitsa.” (2 Timoteyo 3:16) Baibulo limatithandiza kudziŵa zambili zokhudza Mlengi komanso kuti tikhale ndi umoyo wabwino.

Baibulo limati: “Kuti anthu adziŵe kuti inu, amene dzina lanu ndinu Yehova, Inu nokha ndinu Wam’mwambamwamba, wolamulila dziko lonse lapansi.” (Salimo 83:18) Conco, timalambila Yehova Mulungu yekha ndipo monga Mboni zake, timauzako ena za dzina lake.—Yesaya 43:10-12.

Monga Akristu, timakhulupilila kuti Yesu, “Mwana wa Mulungu” * anabwela padziko lapansi n’kukhala Mesiya. (Yohane 1:34, 41; 4:25, 26) Yesu ataphedwa, anaukitsidwa n’kupita kumwamba. (1 Akorinto 15:3, 4) Patapita nthawi anakhala Mfumu ya Ufumu wa Mulungu. (Chivumbulutso 11:15) Ufumu umenewo ndi boma lenileni limene lidzabwezeletsa Paradaiso padziko lapansi. (Danieli 2:44) Baibulo limati: “Koma anthu ofatsa adzalandila dziko lapansi, Ndipo adzasangalala ndi mtendele woculuka.”—Salimo 37:11, 29.

“Akamaŵelenga Baibulo amakhulupilila kuti Mulungu akulankhula nao. Akakumana ndi mavuto amafufuza m’Mau a Mulungu kuti apeze njila yothetsela mavutowo. . . . Kwa io Mau a Mulungu ndi amphamvu.”—Anatelo Benjamin Cherayath, Papa wa chalichi ca katolika m’nyuzipepala ya Münsterländische Volkszeitung ya ku Germany

Mboni za Yehova zimakhulupilila kuti mfundo za m’Baibulo n’zopindulitsa. (Yesaya 48:17, 18) Conco, timatsatila kwambili mfundo zimenezo. Mwacitsanzo, Baibulo limaticenjeza pa zinthu zimene zingaononge maganizo ndi matupi athu. Conco, timapewa kukoka fodya kapena kuseŵenzetsa mankhwala osokoneza bongo. (2 Akorinto 7:1) Timapewanso zinthu zimene Baibulo limaletsa, monga kuledzela, ciwelewele, ndi kuba.—1 Akorinto 6:9-11.

^ par. 4 Baibulo limacha Yesu kuti “Mwana wobadwa yekha wa Mulungu” cifukwa analengedwa mwacindunji ndi Yehova.—Yohane 3:18; Akolose 1:13-15.