NYIMBO 135
Yehova Alangiza Mwacikondi Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzelu”
(Miyambo 27:11)
-
1. Anyamata na ‘tsikana,
nimveleni—
Mdani wanga
wonitonzayo aone
Kuti mun’tumikila
na mtima wonse.
Onetsani onse
kuti munikonda.
(KOLASI)
Ana anga nikukondani.
Inu khalani anzelu.
Sankhani kunitumikila
Ndipo nidzasangalala.
-
2. Muzisangalala
ponitumikila.
Mukalakwa
n’dzakukhululukilani.
Olo kuti ena
sangakukondeni,
Ine Atate wanu
nikukondani.
(KOLASI)
Ana anga nikukondani.
Inu khalani anzelu.
Sankhani kunitumikila
Ndipo nidzasangalala.
(Onaninso Deut. 6:5; Mlal. 11:9; Yes. 41:13)