Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 135

Yehova Alangiza Mwacikondi Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzelu”

Yehova Alangiza Mwacikondi Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzelu”

(Miyambo 27:11)

  1. 1. Anyamata na ‘tsikana,

    nimveleni—

    Mdani wanga

    wonitonzayo aone

    Kuti mun’tumikila

    na mtima wonse.

    Onetsani onse

    kuti munikonda.

    (KOLASI)

    Ana anga nikukondani.

    Inu khalani anzelu.

    Sankhani kunitumikila

    Ndipo nidzasangalala.

  2. 2. Muzisangalala

    ponitumikila.

    Mukalakwa

    n’dzakukhululukilani.

    Olo kuti ena

    sangakukondeni,

    Ine Atate wanu

    nikukondani.

    (KOLASI)

    Ana anga nikukondani.

    Inu khalani anzelu.

    Sankhani kunitumikila

    Ndipo nidzasangalala.

(Onaninso Deut. 6:5; Mlal. 11:9; Yes. 41:13)