Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 28

Kukhala Bwenzi la Yehova

Kukhala Bwenzi la Yehova

(Salimo 15)

  1. 1. Ndani angakhale

    Bwenzi lanu M’lungu?

    Ndani mungakhulupilile?

    Angakudziŵeni?

    Ni uja amene

    Amakumvelani.

    Komanso wokhulupilika,

    Wokonda co’nadi.

  2. 2. Ndani angakhale

    Bwenzi lanu M’lungu?

    Ndani amene mungakonde

    Nakumudalitsa?

    Ni uja amene

    Amakukwezani.

    Iye amanena zoona,

    Ni woona mtima.

  3. 3. Nkhawa zathu zonse

    Timakuuzani.

    Ndipo mumatisamalila,

    Tsiku lililonse.

    Tifuna kukhala

    Bwenzi lanu M’lungu.

    Palibe bwenzi tingapeze

    Monga inu M’lungu.

(Onaninso Sal. 139:1; 1 Pet. 5:6, 7.)