NYIMBO 74
Imbani Nafe Nyimbo ya Ufumu!
(Salimo 98:1)
-
1. Nyimbo iyi ni yacisangalalo;
Imakweza Yehova Mulungu.
Mau ake amatilimbikitsa.
Capamodzi bwelani tiimbe.
(KOLASI)
‘Lambilani M’lungu wathu.
Dziŵitsani anthu onse
Kuti Yesu ndiye alamulila;
Tamandani Yehova Mulungu.’
-
2. Na nyimboyi tilengeza Ufumu:
“Khristu Yesu tsopano ni mfumu.”
Ndipo mtundu watsopano wabadwa;
Nawo udzalamulila naye.
(KOLASI)
‘Lambilani M’lungu wathu.
Dziŵitsani anthu onse
Kuti Yesu ndiye alamulila;
Tamandani Yehova Mulungu.’
-
3. Odzicepetsa angaiphunzile.
Mau ake ni otsitsimula.
M’dziko lonse ambili aphunzila,
Ndipo nawo aitana ena:
(KOLASI)
‘Lambilani M’lungu wathu.
Dziŵitsani anthu onse
Kuti Yesu ndiye alamulila;
Tamandani Yehova Mulungu.’
(Onaninso Sal. 95:6; 1 Pet. 2:9, 10; Chiv. 12:10.)