Onani zimene zilipo

Kodi Niyenela Kupemphela kwa Oyela Mtima?

Kodi Niyenela Kupemphela kwa Oyela Mtima?

Yankho la m’Baibo

 Ayi. Baibo imaonetsa kuti tiyenela kupemphela kwa Mulungu yekha, m’dzina la Yesu. Yesu anauza ophunzila ake kuti: “Cifukwa cake pemphelani inu comweci: Atate wathu wa Kumwamba, Dzina lanu liyeletsedwe.” (Mateyu 6:9, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Iye sanalangizepo ophunzila ake kuti azipemphela kwa oyela mtima, angelo, kapena munthu wina aliyense, koma kwa Mulungu cabe.

 Yesu anauzanso ophunzila ake kuti: “Ine ndine njila, coonadi ndi moyo. Palibe amene amafika kwa Atate osadzela mwa ine.” (Yohane 14:6) Ndipo Mulungu anasakha Yesu yekha kuti tizipeleka mapemphelo athu kupitila mwa iye.—Aheberi 7:25.

Nanga bwanji ngati nimapemphela kwa Mulungu komanso kwa oyela mtima?

 Mu Malamulo Khumi amene Mulungu anapatsa anthu ake, iye anakamba kuti: “Ine Yehova Mulungu wako ndili Mulungu wansanje.” (Ekisodo 20:5,) Kodi Mulungu ni “wansanje” m’njila yotani? Iye amafuna kuti tizilambila iye yekha na kudzipeleka kwa iye. Komanso, amafuna kuti tizipemphela kwa iye yekhabasi.—Yesaya 48:11.

 Conco, timalakwila Mulungu ngati tipemphela kwa munthu winawake, ngakhale oyela mtima, kapenanso angelo oyela. Pamene mtumwi Yohane anafuna kulambila mngelo, mngeloyo anam’letsa n’kumuuza kuti: “Usatelo ayi! Inetu ndangokhala kapolo mnzako, ndi wa abale ako amene ali ndi nchito yocitila umboni za Yesu. Lambila Mulungu”—Chivumbulutso 19:10.