NSANJA YA OLONDA (YOPHUNZIRA) January 2013

Magazini ino ikufotokoza za anthu otchulidwa m’Baibulo omwe anasonyeza kuti anali ndi chikhulupiriro komanso olimba mtima.

Anadzipereka ndi Mtima Wonse ku Norway

Kodi funso limene anafunsidwa mosayembekezereka linathandiza bwanji banja lina kuti lisamukire kudera limene kukufunika anthu ambiri ogwira ntchito yolalikira?

Ukhale Wolimba Mtima Chifukwa Yehova Ali Nawe

Mungapindule ndi zitsanzo za Yoswa, Yehoyada, Danieli ndi anthu ena omwe anasonyeza chikhulupiriro komanso kulimba mtima.

Musalole Chilichonse Kusokoneza Ubwenzi Wanu ndi Yehova

Werengani kuti mudziwe mmene tingasankhire zinthu mwanzeru pa nkhani ya ntchito, zosangalatsa komanso banja lathu.

Pitirizani Kuyandikira Yehova

Kodi tingatani kuti zinthu monga zipangizo zamakono, thanzi, ndalama komanso kunyada zitalilepheretse kukhala pa ubwenzi ndi Yehova?

Tumikirani Yehova Popanda Kunong’oneza Bondo

Pa moyo wake, mtumwi Paulo anapanga zinthu zabwino komanso zinthu zina zimene ananong’oneza nazo bondo. Kodi tingaphunzire chiyani pa zimene zinachitika pa moyo wake?

Akulu Achikhristu Ndi Antchito Anzathu Otipatsa Chimwemwe

Kodi akulu amathandiza bwanji abale ndi alongo kuti azitumikira Mulungu mosangalala?

Anabala Zipatso Chifukwa Chokonzekera Bwino

Werengani kuti mudziwe mmene mtsikana wina wazaka 10 ku Chile anagwirira ntchito mwakhama kuti aitanire aliyense ku sukulu kwake amene amalankhula chinenero cha Chimapudunguni ku mwambo wofunika kwambiri.