NSANJA YA OLONDA (YOPHUNZIRA) January 2013
Magazini ino ikufotokoza za anthu otchulidwa m’Baibulo omwe anasonyeza kuti anali ndi chikhulupiriro komanso olimba mtima.
Anadzipereka ndi Mtima Wonse ku Norway
Kodi funso limene anafunsidwa mosayembekezereka linathandiza bwanji banja lina kuti lisamukire kudera limene kukufunika anthu ambiri ogwira ntchito yolalikira?
Ukhale Wolimba Mtima Chifukwa Yehova Ali Nawe
Mungapindule ndi zitsanzo za Yoswa, Yehoyada, Danieli ndi anthu ena omwe anasonyeza chikhulupiriro komanso kulimba mtima.
Musalole Chilichonse Kusokoneza Ubwenzi Wanu ndi Yehova
Werengani kuti mudziwe mmene tingasankhire zinthu mwanzeru pa nkhani ya ntchito, zosangalatsa komanso banja lathu.
Pitirizani Kuyandikira Yehova
Kodi tingatani kuti zinthu monga zipangizo zamakono, thanzi, ndalama komanso kunyada zitalilepheretse kukhala pa ubwenzi ndi Yehova?
Tumikirani Yehova Popanda Kunong’oneza Bondo
Pa moyo wake, mtumwi Paulo anapanga zinthu zabwino komanso zinthu zina zimene ananong’oneza nazo bondo. Kodi tingaphunzire chiyani pa zimene zinachitika pa moyo wake?
Akulu Achikhristu Ndi Antchito Anzathu Otipatsa Chimwemwe
Kodi akulu amathandiza bwanji abale ndi alongo kuti azitumikira Mulungu mosangalala?
Anabala Zipatso Chifukwa Chokonzekera Bwino
Werengani kuti mudziwe mmene mtsikana wina wazaka 10 ku Chile anagwirira ntchito mwakhama kuti aitanire aliyense ku sukulu kwake amene amalankhula chinenero cha Chimapudunguni ku mwambo wofunika kwambiri.