Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 100

Alandireni Bwino

Alandireni Bwino

(Machitidwe 17:7)

  1. 1. Yehova ndi M’lungu wopanda tsankho.

    Amasamalira mosakondera.

    Amatipatsatu

    Kuwala ndi mvula,

    Amatipatsanso chakudya.

    Timatsanzira Yehova Mulungu

    Ngati tikuthandiza osauka.

    Adzatidalitsa

    Tikamasonyeza

    Anthu onse kukoma mtima.

  2. 2. Pothandiza ena sitingadziwe.

    Madalitso omwe tingalandire.

    Ngakhale ndi oti

    Sitikuwadziwa,

    Tiwapatse zosowa zawo.

    Monga Lidiya wa m’nthawi yakale,

    Akabwera kwathu tiwalandire.

    M’lungu amaona

    Tikamutsanzira

    Pochitira anthu chifundo.