Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 18

Tikuthokoza Chifukwa cha Dipo

Tikuthokoza Chifukwa cha Dipo

(Luka 22:20)

  1. 1. Tsopano tabwera

    Kwa inu Yehova

    Chifukwa munatisonyezadi

    Chikondi.

    Munapereka Mwana

    Wanu woyamba

    Monga nsembe yoposa ina

    Iliyonse.

    (KOLASI)

    Anafera anthu tonse

    Kuti tidzapulumuke.

    Tikuthokoza ndi mtima wonse

    Inu M’lungu.

  2. 2. Mofunitsitsa Yesu

    Anapereka.

    Nsembe ya dipo ndipo

    Tikusangalala.

    Asanabwere

    Kudzapereka dipo,

    Sitinkayembekezera

    Moyo wosatha.

    (KOLASI)

    Anafera anthu tonse

    Kuti tidzapulumuke.

    Tikuthokoza ndi mtima wonse

    Inu M’lungu.