Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 28

Tikhale pa Ubwenzi Ndi Yehova

Tikhale pa Ubwenzi Ndi Yehova

(Salimo 15)

  1. 1. Ndani angakhale

    bwenzi lanu M’lungu?

    Ndani mungam’khulupirire,

    angakhale mnzanu?

    Ndi onse amene

    amakudziwani,

    Amakukhulupirirani,

    amakukondani.

  2. 2. Ndani angakhale

    bwenzi lanu M’lungu?

    Ndani angafike kumpando

    wanu wachifumu?

    Ndi onse amene

    Amakumverani,

    Olemekeza dzina lanu,

    Okulambirani.

  3. 3. Timakuuzani

    Zamumtima mwathu.

    Mumakhala nafe pafupi

    Mumatithandiza.

    Tikufunitsitsa

    Kukhala anzanu

    Ndipo palibe bwenzi

    Lomwe lingakuposeni.