Pitani ku nkhani yake

Kodi Mumakhulupirira Kuti Chipembedzo Cholondola N’chanu Chokha?

Kodi Mumakhulupirira Kuti Chipembedzo Cholondola N’chanu Chokha?

 Anthu amene amakonda kwambiri za chipembedzo ayenera kukhulupirira kuti Mulungu ndiponso Yesu amavomereza chipembedzo chawo. Ngati sakhulupirira kuti chipembedzo chawo n’cholondola ndiye kuti palibe chifukwa chokhalira m’chipembedzocho.

 Yesu Khristu sanavomereze maganizo akuti pali zipembedzo zambiri, kapena kuti misewu yambiri yopita kumoyo wosatha. M’malomwake iye anati: “Chipata cholowera ku moyo n’chopapatiza komanso msewu wake ndi wopanikiza, ndipo amene akuupeza ndi owerengeka.” (Mateyu 7:14) A Mboni za Yehova amakhulupirira kuti anapeza msewu umenewu. Akanakhala kuti sanaupeze akanalowa chipembedzo china.