Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 99

Abale Miyanda Miyanda

Abale Miyanda Miyanda

(Chivumbulutso 7:9,10)

  1. 1. Abale ni myanda myanda,

    Osaŵelengeka,

    Aliyense ni mboni,

    Yokhulupilika.

    Ise ndise ambili,

    Tikuwonjezeka,

    Tacoka kumitundu yonse,

    Titamanda M’lungu.

  2. 2. Ise tili myanda myanda,

    Timalalikila

    Za uthenga wabwino,

    Ku mitundu yonse.

    Olo tileme bwanji,

    Timalalikila,

    Yesu amatitsitsimula;

    Timapeza mphamvu.

  3. 3. Abale ni myanda myanda,

    M’lungu atikonda,

    Iye afuna kuti,

    Tizim’tumikila.

    Mokondwa tilengeza,

    Za Ufumu wake,

    Tikagwila nchito na M’lungu,

    Timasangalala.

(Onaninso Yes. 52:7; Mat. 11:29; Chiv. 7:15.)