Wolembedwa ndi Yohane 7:1-52

  • Yesu anapita ku Chikondwerero cha Misasa (1-13)

  • Yesu anaphunzitsa kuchikondwerero (14-24)

  • Anthu anali ndi maganizo osiyanasiyana okhudza Khristu (25-52)

7  Zimenezi zitatha, Yesu anapitiriza kugwira ntchito yake* mu Galileya. Iye sanafune kuchita zimenezi mu Yudeya chifukwa Ayuda ankafunitsitsa kumupha.+  Koma Chikondwerero cha Misasa cha Ayuda+ chinali chitayandikira.  Ndiye azichimwene ake+ anamuuza kuti: “Mupite ku Yudeya kuti ophunzira anunso akaone zimene mukuchita.  Chifukwa palibe munthu amene amachita zinthu mwachinsinsi pamene akufuna kudziwika kwa anthu. Ngati inu mumachita zinthu zimenezi, mudzionetsere poyera kudzikoli.”  Azichimwene akewo sankamukhulupirira.+  Yesu anawauza kuti: “Nthawi yanga sinafikebe,+ koma kwa inu, nthawi iliyonse imakhala yoyenera.  Dziko lilibe chifukwa choti lizidana nanu, koma limadana ndi ine, chifukwa ndimachitira umboni kuti ntchito zake ndi zoipa.+  Inuyo nyamukani mupite kuchikondwereroko. Ine sindipitako panopa, chifukwa nthawi yanga sinafike.”+  Atawauza zimenezi, iye anatsala ku Galileya. 10  Koma azichimwene akewo atanyamuka kupita kuchikondwereroko, iyenso ananyamuka. Sanapite moonekera koma mwachinsinsi. 11  Ndiyeno Ayuda anayamba kumufunafuna kuchikondwereroko. Iwo ankanena kuti: “Kodi munthu ujayu ali kuti?” 12  Ndipo anthu ankanena zinthu zambirimbiri zokhudza iyeyo mʼgulu lonselo. Ena ankanena kuti: “Amene uja ndi munthu wabwino.” Koma ena ankanena kuti: “Ayi si munthu wabwino amene uja. Iye akusocheretsa anthu ambiri.”+ 13  Koma panalibe amene ankalankhula poyera zokhudza iye chifukwa ankaopa Ayuda.+ 14  Chikondwererocho chitafika pakatikati, Yesu analowa mʼkachisi ndipo anayamba kuphunzitsa. 15  Ayudawo anadabwa nʼkufunsa kuti: “Kodi munthu ameneyu Malemba+ amenewa anawadziwa* bwanji, popeza sanapite kusukulu?”*+ 16  Yesu anawayankha kuti: “Zimene ine ndimaphunzitsa si zanga, koma ndi za amene anandituma.+ 17  Ngati munthu akufuna kuchita zimene Mulungu amafuna, adzadziwa ngati zimene ndimaphunzitsa zimachokera kwa Mulungu,+ kapena ngati ndimalankhula zamʼmaganizo mwanga. 18  Wolankhula zamʼmaganizo mwake amadzifunira yekha ulemerero. Koma wofunira ulemerero iye amene anamutuma,+ ameneyu ndi woona ndipo mwa iye mulibe chosalungama. 19  Mose anakupatsani Chilamulo,+ si choncho? Komatu palibe ngakhale mmodzi wa inu amene amamvera Chilamulocho. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha?”+ 20  Gulu la anthulo linayankha kuti: “Uli ndi chiwanda iwe. Akufuna kukupha ndi ndani?” 21  Poyankha Yesu anawauza kuti: “Ndangochita chinthu chimodzi chokha ndipo nonsenu mukudabwa. 22  Pa chifukwa chimenechi Mose anakupatsani mdulidwe.+ Sikuti mdulidwewo ndi wochokera kwa Mose ayi, koma ndi wochokera kwa makolo akale,+ ndipo mumachita mdulidwe tsiku la sabata. 23  Ngati munthu amadulidwa tsiku la sabata posafuna kuphwanya Chilamulo cha Mose, kodi mukundipsera mtima kwambiri chifukwa ndinachiritsa munthu tsiku la sabata?+ 24  Siyani kuweruza potengera maonekedwe akunja, koma muziweruza ndi chiweruzo cholungama.”+ 25  Ndiyeno anthu ena okhala mu Yerusalemu anayamba kunena kuti: “Kodi munthu akufuna kumupha uja si ameneyu?+ 26  Koma taonani! Si uyu akulankhula poyerayu ndipo sakumuuza chilichonse. Kodi olamulirawa atsimikiza tsopano kuti iyeyu ndi Khristu? 27  Komatu ife tikudziwa kumene munthu ameneyu akuchokera.+ Komano Khristuyo akadzabwera, palibe amene adzadziwe kumene wachokera.” 28  Ndiyeno akuphunzitsa mʼkachisimo Yesu anafuula kuti: “Inu mukundidziwa komanso mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindinabwere mwa kufuna kwanga,+ koma amene anandituma alipodi ndipo inu simukumudziwa.+ 29  Ine ndikumudziwa,+ chifukwa ndine nthumwi yake. Iyeyo ndi amene anandituma.” 30  Choncho iwo anayamba kufufuza njira yomugwirira,+ koma palibe amene anamugwira chifukwa nthawi yake inali isanafike.+ 31  Komabe anthu ambiri mʼgululo anamukhulupirira+ ndipo ankanena kuti: “Kodi Khristu akadzabwera, adzachita zizindikiro zochuluka kuposa zimene munthu uyu wachita?” 32  Afarisi anamva gulu la anthulo likunongʼonezana zimenezi zokhudza iye ndipo ansembe aakulu komanso Afarisi anatuma alonda kuti akamugwire.* 33  Kenako Yesu ananena kuti: “Ndikhala nanube kanthawi pangʼono ndisanapite kwa iye amene anandituma.+ 34  Mudzandifunafuna koma simudzandipeza, ndipo kumene ndidzapiteko inu simudzatha kukafikako.”+ 35  Choncho Ayudawo anayamba kufunsana kuti: “Kodi munthu ameneyu akufuna kupita kuti, kumene ife sitingathe kumupeza? Kapena akufuna kupita kwa Ayuda amene anamwazikana pakati pa Agiriki nʼkukaphunzitsa Agirikiwo? 36  Kodi akutanthauza chiyani pamene akunena kuti, ‘Mudzandifunafuna koma simudzandipeza, ndipo kumene ine ndidzapite inu simudzatha kukafikakoʼ?” 37  Pa tsiku lomaliza, tsiku lalikulu la chikondwererocho,+ Yesu anaimirira nʼkufuula kuti: “Ngati wina akumva ludzu, abwere kwa ine adzamwe madzi.+ 38  Mogwirizana ndi zimene lemba limanena, aliyense wokhulupirira ine, ‘Mkati mwake mwenimwenimo mudzatuluka mitsinje ya madzi amoyo.’”+ 39  Pamenepa ankanena za mzimu umene onse amene anamukhulupirira anali atatsala pangʼono kulandira. Pa nthawiyi nʼkuti anthu asanalandire mzimu+ chifukwa Yesu anali asanalandire ulemerero wake.+ 40  Ena mʼgululo amene anamva mawu amenewa, anayamba kunena kuti: “Ndithu ameneyu ndi Mneneri.”+ 41  Ena ankanena kuti: “Khristu uja ndi ameneyu.”+ Koma ena ankati: “Kodi Khristu angachokere mu Galileya?+ 42  Kodi si paja lemba limanena kuti Khristu adzachokera mwa ana a Davide+ komanso ku Betelehemu,+ mudzi umene Davide ankakhala?”+ 43  Choncho gulu la anthulo linagawanika pa nkhani yokhudza iye. 44  Ena a iwo ankafuna kumugwira,* koma palibe ngakhale mmodzi amene anamukhudza. 45  Kenako alonda aja anabwerera kwa ansembe aakulu ndi Afarisi ndipo iwo anawafunsa kuti: “Nʼchifukwa chiyani simunabwere naye?” 46  Alondawo anayankha kuti: “Palibe munthu amene analankhulapo ngati iyeyu nʼkale lonse.”+ 47  Ndiyeno Afarisiwo anati: “Kodi inunso mwasocheretsedwa? 48  Palibe ndi mmodzi yemwe mwa olamulira kapena Afarisi amene akumukhulupirira, alipo ngati?+ 49  Koma gulu lonse la anthu osadziwa Chilamulowa ndi lotembereredwa.” 50  Nikodemo, amene mʼmbuyomo anapita kwa Yesu, komanso anali mmodzi wa Afarisi, anawauza kuti: 51  “Chilamulo chathu sichiweruza munthu asanafotokoze maganizo ake choyamba nʼkudziwa zimene akuchita, chimatero ngati?”+ 52  Poyankha iwo anamuuza kuti: “Kodi iwenso ndiwe wochokera ku Galileya eti? Fufuza ndipo supeza pamene pamati mʼGalileya mudzatuluka mneneri.”*

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “anapitiriza kuyendayenda.”
Imeneyi ndi sukulu ya Arabi.
Mʼchilankhulo choyambirira, “zolembedwazi anazidziwa.”
Kapena kuti, “akamumange.”
Kapena kuti, “kumumanga.”
Mipukutu ina yakale komanso yodalirika inachotsa vesi 53 mpaka chaputala 8 vesi 11.