Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI N’ZOTHEKA KUMVETSA ZIMENE BAIBULO LIMANENA?

Baibulo Ndi Buku Lothandiza Kwambiri

Baibulo Ndi Buku Lothandiza Kwambiri

Mayi wina wa ku China, dzina lake Lin anati: “Ndimadziwa ndithu kuti Baibulo ndi buku limene anthu ambiri opemphera amaligwiritsa ntchito koma ndimaona kuti ndi lothandiza m’mayiko ena osati ku China kuno.”

Bambo wina wa ku India, dzina lake Amit, ananena kuti: “Ngati ndimalephera kumvetsa mabuku a chipembedzo changa chachihindu, ndiye kuli bwanji Baibulo?”

Mayi wina wa ku Japan, dzina lake Yumiko anati: “Ndimangomva zoti Baibulo ndi buku lakale komanso kuti anthu ambiri ali nalo. Koma chibadwire sindinalionepo.”

Padzikoli anthu ambiri ali ndi Baibulo ndipo amaona kuti ndi lofunika. Ngakhale zili choncho, anthu ambiri a m’mayiko a ku Asia amadziwa zochepa kwambiri ndipo ena sadziwa n’komwe zimene Baibulo limanena. Ndipo n’zodabwitsanso kwambiri kuti m’mayiko omwe Baibulo ndi buku lofala kwambiri, anthu owerengeka chabe ndi amene amadziwa zimene limanena.

Ndiye mwina mungafunse kuti, ‘Kodi kudziwa zimene Baibulo limanena kungandithandize bwanji?’ Kumvetsa zimene Baibulo limanena kungakuthandizeni:

  • Kudziwa zimene mungachite kuti muzisangalala

  • Kukhala ndi banja losangalala

  • Kuti musakhale ndi nkhawa

  • Kuti muzigwirizana ndi anthu ena

  • Kuti muzitha kugwiritsa ntchito bwino ndalama

Mayi wina wa ku Japan, dzina lake Yoshiko, ankafuna kudziwa zimene Baibulo limaphunzitsa ndipo anaganiza zongoliwerenga yekha. Kodi zotsatira zake zinali zotani? Yoshiko anati: “Baibulo landithandiza kudziwa chifukwa chake Mulungu anatilenga komanso zimene tikuyembekezera kutsogoloku. Zimenezi zandithandiza kuti ndizisangalala.” Nayenso Amit amene tamutchula poyamba uja anawerenga Baibulo payekha ndipo ananena kuti: “Nditawerenga Baibulo ndinadabwa nditadziwa kuti ndi buku lothandiza wina aliyense.”

Baibulo lathandiza anthu mamiliyoni ambiri. Inunso lingakuthandizeni ngati mutaliwerenga ndi kumvetsa zimene limanena.