Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 129

Tipitirizebe Kupirira

Tipitirizebe Kupirira

(Mateyu 24:13)

  1. 1. Tizipirira

    Mayesero ngati Yesu.

    Anavutika

    Koma ankasangalala

    Ndi chiyembekezo.

    Analimba mtima.

    (KOLASI)

    Tikhale opirira.

    Tizilalikira.

    M’lungu amatikonda

    Adzatithandiza kupirira.

  2. 2. Tingakumane

    Ndi mavuto ochuluka,

    Tidikirebe

    Moyo wosatha m’tsogolo.

    Tikulakalaka

    Mtendere wosatha.

    (KOLASI)

    Tikhale opirira.

    Tizilalikira.

    M’lungu amatikonda

    Adzatithandiza kupirira.

  3. 3. Sitimaopa

    Kapena kukayikira.

    Titumikire

    Mpaka tsiku lomaliza.

    Tsiku la Yehova

    Lilidi pafupi.

    (KOLASI)

    Tikhale opirira.

    Tizilalikira.

    M’lungu amatikonda

    Adzatithandiza kupirira.